14. Popeza tsono tiri naye Mkuluwansembe wamkuru, wopyoza miyamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tigwiritsitse cibvomerezo cathu.
15. Pakuti sitiri naye mkulu wa ansembe wosatha kumva cifundo ndi zofoka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda ucimo.
16. Potero tilimbike mtima poyandikira mpando wacifumu wacisomo, kuti tilandire cifundo ndi kupeza cisomo ca kutithandiza nthawi yakusowa.