Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 3:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. komatu dandauliranani nokha tsiku ndi tsiku, pamene paehedwa, Lero; kuti angaumitsidwe wina wa inu ndi cenjerero la ucimo;

14. pakuti takhala ife olandirana ndi Kristu, ngatitu tigwiritsa ciyambi ca kutama kwathu kucigwira kufikira citsiriziro;

15. umo anenamo,Lero ngati mudzamva mau ace,Musaumitse mitima yanu, monga pa kupsetsa mtima.

16. Pakuti ndi ayani, pakumva, anapsetsa mtima? Kodi si onse aja adaturuka m'Aigupto ndi Mose?

17. Koma anakwiya ndi ayani zaka makumi anai? Kodi si ndi awo adacimwawo, amene matupi ao adagwa m'cipululu?

18. Ndipo adawalumbirira ayani kuti asalowe mpumulo wace?

19. Si awo kodiosamverawo? Ndipo tiona kuti sanakhoza kulowa cifukwa ca kusakhulupirira.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 3