Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 3:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Potero, abale oyera mtima, olandirana nao maitanidwe akumwamba, lingirirani za Mtumwi ndi. Mkuluwansembe wa cibvomerezo cathu, Yesu;

2. amene anakhala wokhulupirika kwa iye adamuikayo, monganso Mose m'nyumba yace yonse.

3. Pakuti ameneyo wayesedwa woyenera ulemerero woposa Mose, monga momwe iye amene anaimanga nyumba ali nao ulemerero woposa nyumbayi.

4. Pakuti nyumba iri yonse iri naye wina woimanga; koma wozimanga zonse ndiye Mulungu.

5. Ndipo Mosetu anali wokhulupirika m'nyumba yace yonse, monga mnyamata, acitire umboni izi zidzalankhulidwazi;

Werengani mutu wathunthu Ahebri 3