Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 13:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo ndikudandaulirani koposa kucita ici, kuti kubwera kwanga kwa inu kufulumidwe.

20. Koma Mulungu wa mtendere amene anabwera naye woturuka mwa akufa 1 Mbusa wamkuru wa nkhosa 2 ndi mwazi wa cipangano cosatha, ndiye Ambuye wathu Yesu,

21. 3 akuyeseni inu opanda cirema m'cinthu ciri conse cabwino, kuti mucite cifuniro cacej ndi kucita mwa ife comkondweretsa pamaso pace, mwa Yesu Kristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero ku nthawi za nthawi. Amen.

22. Koma ndidandaulira inu, abale, lolani mau acidandauliro; pakutinso ndalembera inu mwacidule.

23. Zindikirani kuti mbale wathu 4 Timoteo wamasulidwa; pamodzi ndi iye, ngati akudza msanga, ndidzakuonani inu.

24. Lankhulani 5 atsogoleri anu onse, ndi oyera mtima onse. Akulankhulani iwo a ku Italiya.

25. Cisomo cikhale ndi inu nonse. Amen.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 13