Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 13:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cikondi ca pa abale cikhalebe.

2. Musaiwale kucereza alendo; pakuti mwa ici ena anacereza angelo osacidziwa.

3. Kumbukilani am'nsinga, monga am'nsinga anzao; ocitidwa zoipa, monga ngati inunso adatero nanu m'thupi.

4. Ukwati ucitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi acigololo adzawaweruza Mulungu.

5. Mtima wanu ukhale wosakonda cuma; zimene muli nazo zikukwanireni; pakuti iye anati, Sindidzakusiya konse, kungakhale kukutaya, sindidzakutaya ndithu.

6. Kotero kuti tinena molimbika mtima,Mthandizi wanga ndiye Ambuye; smdidzaopa;Adzandicitira ciani munthu?

7. Kumbukilani atsogoleri anu, amene analankhula nanu Mau a Mulungu; ndipo poyang'anira citsiriziro ca mayendedwe ao mutsanze cikhulupiriro cao.

8. Yesu Kristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi ku nthawi zonse.

9. Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundu mitundu, ndi acilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi cisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo.

10. Tiri nalo guwa la nsembe, limene iwo akutumikira cihema alibe ulamuliro wa kudyako.

11. Pakuti matupi a nyama zija, mwazi wa izo umatengedwa ndi mkulu wa ansembe kulowa m'malo opatulidwa, cifukwa ca zoipa, amatenthedwa kunja kwa tsasa.

12. Mwa ici Yesunso, kuti akayeretse anthuwo mwa mwazi wa iye yekha, adamva cowawa kunja kwa cipata.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 13