3. Pakuti talingirirani iye amene adapirira ndi ocimwa otsutsana naye kotere, kuti mungaleme ndi kukomoka m'moyo mwanu.
4. Simunakana kufikira mwazi pogwirana nalo cimo;
5. ndipo mwaiwala dandauliro limene linena nanu monga ndi ana,Mwana wanga, usayese copepuka kulanga kwa Ambuye,Kapena usakomoke podzudzulidwa ndilye;
6. Pakuti iye amene Ambuye amkonda amlanga,Nakwapula mwana ali yense amlandira.
7. Mukapirira kufikira kulangidwa Mulungu acitira inu monga ngati ana; pakuti mwana wanji amene atate wace wosamlanga?
8. Koma ngati mukhala opanda cilango, cimene onse adalawako, pamenepo muli am'thengo, si ana ai.
9. Komanso, tinali nao atate a thupi lathu akutilanga, ndipo tinawalemekeza; kodi sitidzagonjera Atate wa mizimu koposa nanga, ndi kukhala ndi moyo?
10. Pakutitu iwo anatilanga masiku owerengeka monga kudawakomera; koma iye atero, kukatipindulitsa, kuti tikalandirane nao pa ciyero cace.
11. Chango ciri conse, pakucitika, sicimveka cokondwetsa, komatu cowawa; koma citatha, cipereka cipatso ca mtendere, kwa iwo ozoloweretsedwa naco, ndico ca cilungamo.
12. Mwa ici limbitsani manja ogooka, ndi maondo olobodoka;
13. ndipo lambulani miseu yolunjika yoyendamo mapazi anu, kuti cotsimphinaco cisapatulidwe m'njira, koma ciciritsidwe.
14. Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi ciyeretso cimene, akapanda ici, palibe mmodzi adzaona Ambuye: