27. koma kulindira kwina koopsa kwa ciweruziro, ndi kutentha kwace kwa mota wakuononga otsutsana nao.
28. Munthu wopeputsa cilamulo ca Mose angofa opanda cifundo pa mboni ziwiri kapena zitatu:
29. ndipo mutani, kulanga koposa kotani nanga adzayesedwa woyenera iye amene anapondereza Mwana wa Mulungu, nayesa mwazi wa cipangano umene anayeretsedwa nao cinthu wamba, z nacitira cipongwe Mzimu wa cisomo;
30. pakuti timdziwa iye amene anati, 1 Kubwezera cilango nkwanga, loe ndidzabwezera. Ndiponso; 2 Ambuye adzaweruza anthu ace.
31. 3 Kugwa m'manja a Mulungu wamoyo nkoopsa.
32. Koma tadzikumbursani masiku akale, m'menemo mutaunikidwa 4 mudapirira citsutsano cacikuru ca zowawa;
33. pena pocitidwa 5 cinthu cooneredwa mwa matonzo ndi zisautso; penanso polawana nao iwo ocitidwa zotere.