Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 10:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. koma iye, m'mene adapereka nsembe imodzi cifukwa ca macimo, anakhala pa dzanja lamanja la Mulungu cikhalire;

13. kuyambira pomwepo alindirira, kufikira adani ace aikidwa akhale mpando ku mapazi ace.

14. Pakuti ndi cipereko cimodzi anawayesera angwiro cikhalire iwo oyeretsedwa.

15. Koma Mzimu Woyeranso aticitira umboni; pakuti adatha kunena,

16. ici ndi cipangano ndidzapangana nao,Atapira masiku ajawo, anena Ambuye:Ndidzapereka malamulo anga akhale pamtima pao;Ndipo pa nzeru zao ndidzawalemba;

17. Ndipo macimo ao ndi masayeruziko ao sindidzawakumbukilanso.

18. Koma pomwe pali cikhululukiro ca macimo palibenso copereka ca kwaucimo.

19. Ndipo pokhala naco, abale, cilimbikitso cakulowa m'malo opatulika, ndi mwazi wa Yesu,

20. pa njira yatsopano ndi yamoyo, imene adatikonzera, mwa cocinga, ndico thupi lace;

Werengani mutu wathunthu Ahebri 10