Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 10:11-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipotu wansembe ali yenseamaima tsiku ndi tsiku, natumikira, napereka nsembe zomwezi kawiri kawiri, zimene sizikhoza konse kucotsa macimo;

12. koma iye, m'mene adapereka nsembe imodzi cifukwa ca macimo, anakhala pa dzanja lamanja la Mulungu cikhalire;

13. kuyambira pomwepo alindirira, kufikira adani ace aikidwa akhale mpando ku mapazi ace.

14. Pakuti ndi cipereko cimodzi anawayesera angwiro cikhalire iwo oyeretsedwa.

15. Koma Mzimu Woyeranso aticitira umboni; pakuti adatha kunena,

16. ici ndi cipangano ndidzapangana nao,Atapira masiku ajawo, anena Ambuye:Ndidzapereka malamulo anga akhale pamtima pao;Ndipo pa nzeru zao ndidzawalemba;

17. Ndipo macimo ao ndi masayeruziko ao sindidzawakumbukilanso.

18. Koma pomwe pali cikhululukiro ca macimo palibenso copereka ca kwaucimo.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 10