Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 4:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. koma mwenzi nditakhala nanu tsopano, ndi kusintha mau anga; cifukwa ndisinkhasinkha nanu.

21. Ndiuzeni, inu akufuna kukhala omvera lamulo, kodi simukumva cilamulo?

22. Pakuti palembedwa, kuti Abrahamu anali nao ana amuna awiri, mmodzi wobadwa mwa mdzakazi, ndi mmodzi wobadwa mwa mfulu.

23. Komatu uyo wa mdzakazi anabadwa monga mwa thupi; koma iye wa mfuluyo, anabadwa monga mwa Ionjezano, Izo ndizo zophiphiritsa;

24. pakuti akaziwa ali mapangano awiri, mmodzi wa ku phiri la Sinai, akubalira ukapolo, ndiye Hagara.

25. Koma Hagara ndiye phiri la Sinai, m'Arabiya, nafanana ndi Yerusalemu wa tsopano; pakuti ali muukapolo pamodzi ndi ana ace.

26. Koma, Yerusalemu wa kumwamba uli waufulu, ndiwo amai wathu.

27. Pakuti kwalembedwa,Kondwera, cumba iwe wosabala;Yimba nthungululu, nupfuule iwe wosamva kuwawa kwa kubala;Pakuti ana ace a iye ali mbeta acuruka koposa ana a iye ali naye mwamuna.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 4