Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 4:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma ndinena kuti, pokhala wolowa nyumba ali wakhanda, sasiyana ndi kapolo, angakhale ali mwini zonse;

2. komatu ali wakumvera omsungira ndi adindo, kufikira nthawi yoikika kale ndi atate wace.

3. Koteronso ife, pamene tinali akhanda, tinali akapolo akumvera miyambo ya dziko lapansi;

4. koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wace, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,

5. kuti akaombole iwo akumvera lamulo, kuti ife tikalandire umwana.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 4