Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 3:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. cotero zindikirani kuti iwo a cikhulupiriro ndiwo ana a Abrahamu.

8. Ndipo malembo, pakuoneratu kuti Mulungu adzayesa olungama amitundu ndi cikhulupiriro, anayamba kale kulalikira Uthenga Wabwino kwa Abrahamu, kuti, Idzadalitsidwa mwa iwe mitundu yonse.

9. Kotero kuti iwo a cikhulupiriro adalitsidwa pamodzi ndi Abrahamu wokhulupirikayo,

10. Pakuti onse amene atama nchito za lamulo Iiwakhalira temberero; pakuti kwalembedwa,Wotembereredwa ali yense wosakhala m'zonse zolembedwa m'buku la cilamulo, kuzicita izi.

11. Ndipo cidziwikatu kuti palibe munthu ayesedwa wolungama ndi lamulo pamaso pa Mulungu; pakuti, Wolungama adzakhala ndi moyo ndi cikhulupiriro;

12. koma cilamulo sicicokera kucikhulupiriro; koma, Wakuzicita izi adzakhala ndi moyo ndi izi.

13. Kristu anatiombola ku temberero la cilamulo, atakhala temberero m'malo mwathu; pakuti kwalembedwa,Wotembereredwa ali yense woo paeikidwa pamtengo;

14. kutidalitso la Abrahamu mwa Yesu Kristu, licitike kwa amitundu; kuti tikalandire lonjezano la Mzimuyo, mwa cikhulupiriro.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 3