Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 3:23-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Koma cisanadze cikhulupiriro tinasungidwa pomvera lamulo otsekedwa kufikira cikhulupiriro cimene cikabvumbulutsidwa bwino bwino.

24. 1 Momwemo cilamulo cidakhala namkungwi wathu wakutifikitsa kwa Kristu, 2 kuti tikayesedwe olungama ndi cikhulupiriro.

25. Koma popeza cadza cikhulupiriro, sitikhalanso omvera namkungwi.

26. 3 Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa cikhulupiriro ca mwa Yesu Kristu.

27. 4 Pakuti nonse amene munabatizidwa kwa Kristu mudabvala Kristu.

28. 5 Muno mulibe Myuda, kapena Mhelene, muno mulibe kapolo, kapena mfulu, muno mulibe mwamuna ndi mkazi; 6 pakuti muli nonse mmodzi mwa Kristu Yesu.

29. Koma ngati muli a Kristu, muli mbeu ya Abrahamu, 7 nyumba monga mwa Lonjezano.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 3