Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 1:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma ngakhale ife, kapena mngelo wocokera Kumwamba, ngati akakulalikireni uthenga wabwino wosati umene tidakulalikirani ife, akhale wotembereredwa.

9. Monga tinanena kale, ndipo ndinenanso tsopano apa, ngati wina akulalikirani uthenga wabwino wosati umene mudaulandira, akhale wotembereredwa.

10. Pakuti kodi ndikopa anthu tsopano, kapena Mulungu? Kapena kodi ndifuna kukondweretsa anthu? Ndikadakhala wokondweretsabe anthu, sindikadakhala kapolo wa Kristu.

11. Pakuti ndikudziwitsani inu, abale, za Uthenga Wabwinowo wolalikidwa ndi ine, kuti suli monga mwa anthu.

12. Pakutitu sindinaulandira kwa munthu, kapena sindinauphunzira, komatu unadza mwa bvumbulutso la Yesu Kristu.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 1