Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 4:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Koma ndiri nazo zonse, ndipo ndisefukira; ndadzazidwa, popeza ndalandira kwa Epafrodito zija zidacokera kwanu, mnunkho wa pfungo labwino, nsembe yolandirika, yokondweretsa Mulungu.

19. Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa cosowa canu ciri conse monga mwa cuma cace m'ulemerero mwa Kristu Yesu.

20. Ndipo kwa Mulungu ndi Atate wathu kukhale ulemerero ku nthawi za nthawi, Amen.

21. Lankhulani woyera mtima ali yense mwa Kristu Yesu. Abalewo akukhala ndiine alankhula inu.

22. Oyera mtima onse alankhula inu, koma makamaka-fwo a banja la Kaisara.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 4