Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 4:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. pakuti m'Tesalonikanso munanditumizira pa cosowa canga kamodzi kapena kawiri.

17. Sikunena kuti nditsata coperekaco, komatu nditsata cipatsocakucurukira ku ciwerengero canu.

18. Koma ndiri nazo zonse, ndipo ndisefukira; ndadzazidwa, popeza ndalandira kwa Epafrodito zija zidacokera kwanu, mnunkho wa pfungo labwino, nsembe yolandirika, yokondweretsa Mulungu.

19. Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa cosowa canu ciri conse monga mwa cuma cace m'ulemerero mwa Kristu Yesu.

20. Ndipo kwa Mulungu ndi Atate wathu kukhale ulemerero ku nthawi za nthawi, Amen.

21. Lankhulani woyera mtima ali yense mwa Kristu Yesu. Abalewo akukhala ndiine alankhula inu.

22. Oyera mtima onse alankhula inu, koma makamaka-fwo a banja la Kaisara.

23. Cisomo ca Ambuye Yesu Kristu cikhale ndi mzimu wanu.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 4