Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 6:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. kuti kukhale bwino ndi iwe, ndi kuti ukhale wa nthawi yaikuru padziko.

4. Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi cilangizo ca Ambuye.

5. Akapolo inu, mverani iwo amene ali ambuye anu monga mwa thupi, ndi kuwaopa ndi kunthunthumira nao, ndi mtima wanu wosakumbukila kanthu kena, monga kwa Kristu;

6. si monga mwa ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu monga akapolo a Kristu, akucita cifuniro ca Mulungu cocokera kumtima;

7. akucita ukapolo ndi kubvomereza mtima, monga kutumikira Yesu Kristu, si anthu ai;

Werengani mutu wathunthu Aefeso 6