Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 6:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. mwa pemphero lonse ndi pembedzero mupemphere nthawi yonse mwa Mzimu, ndipo poeezera pamenepo cicezerere ndi kupembedzera oyera mtima onse,

19. ndi ine ndemwe, kuti andipatse mau m'kunditsegulira m'kamwa molimbika, kuti ndizindikiritse anthu cinsinsico ca Uthenga Wabwino,

20. cifukwa ca umene 1 ndiri mtumiki wa m'unyolo, kuti m'menemo ndikalankhule molimbika, monga ndiyenera kulankhula.

21. Koma 2 kuti mukadziwe inunso za kwa ine, zimene ndicita, zinthu zonse adzakuzindikiritsani Tukiko mbale wokondedwayo, ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye;

22. amene ndamtuma kwa inu cifukwa ca icico, kuti mukazindikire za kwa ife, ndi kuti akatonthoze mitima yanu.

23. 3 Mtendere ukhale kwa abale, ndi cikondi, pamodzi ndi cikhulupiriro, zocokera kwa Mulungu Atate, ndi Ambuye Yesu Kristu.

24. Akhale naco cisomo onse akukonda Ambuye wathu Yesu Kristu m'eosaonongeka.

Werengani mutu wathunthu Aefeso 6