Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 5:9-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. pakuti cipatso ca kuunika ticipeza m'ubwino wonse, ndi cilungamo, ndi coonadi,

10. kuyesera cokondweretsa Ambuye nciani;

11. ndipo musayanjane nazo nchito za mdima zosabala kanthu, koma maka-makanso muzitsutse;

12. pakuti zocitidwa nao m'tseri, kungakhale kuzinena kucititsa manyazi.

13. Koma zinthu zonse potsutsika ndi kuunika, zionekera; pakuti conse cakuonetsa ciri kuunika.

14. Mwa ici anena, Khala maso wogona iwe, nuuke kwa akufa, ndi, po Kristu adzawala pa iwe.

15. Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;

16. akucita macawi, popeza masiku ali oipa,

17. Cifukwa cace musakhale opusa, koma dziwitsani cifuniro ca Ambuye nciani.

18. Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli citayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

19. ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira ndi kuyimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu;

20. ndi kuyamika Mulungu Atate masiku onse, cifukwa ca zonse, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu;

21. ndi kumverana wina ndi mnzace m'kuopa Kristu.

22. Akazi Inu, mverani amuna anu ainu eni, monga kumvera Ambuye.

23. Pakuti mwamuna ndiye mutu wa mkazi, monganso Kristu ndiye mutu wa Eklesia, ali yekha Mpulumutsi wa thupilo.

24. Komatu monga Eklesia amvera Kristu, koteronso akazi amvere amuna ao m'zinthu zonse.

Werengani mutu wathunthu Aefeso 5