Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 5:5-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pakuti ici mucidziwe kuti wadama yense, kapena wacidetso, kapena wosirira, amene apembedza mafano, alibe colowa m'ufumu wa Kristu ndi Mulungu.

6. Asakunyengeni inu munthu ndi mau opanda pace, pakuti cifukwa ca hi umadza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera.

7. Cifukwa cace musakhale olandirana nao;

8. pakuti kale munali mdima, koma tsopano muli kuunika mwa Ambuye; yendani monga ana a kuunika,

9. pakuti cipatso ca kuunika ticipeza m'ubwino wonse, ndi cilungamo, ndi coonadi,

10. kuyesera cokondweretsa Ambuye nciani;

11. ndipo musayanjane nazo nchito za mdima zosabala kanthu, koma maka-makanso muzitsutse;

12. pakuti zocitidwa nao m'tseri, kungakhale kuzinena kucititsa manyazi.

13. Koma zinthu zonse potsutsika ndi kuunika, zionekera; pakuti conse cakuonetsa ciri kuunika.

14. Mwa ici anena, Khala maso wogona iwe, nuuke kwa akufa, ndi, po Kristu adzawala pa iwe.

15. Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;

16. akucita macawi, popeza masiku ali oipa,

17. Cifukwa cace musakhale opusa, koma dziwitsani cifuniro ca Ambuye nciani.

18. Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli citayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

19. ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira ndi kuyimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu;

20. ndi kuyamika Mulungu Atate masiku onse, cifukwa ca zonse, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu;

Werengani mutu wathunthu Aefeso 5