Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 5:11-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. ndipo musayanjane nazo nchito za mdima zosabala kanthu, koma maka-makanso muzitsutse;

12. pakuti zocitidwa nao m'tseri, kungakhale kuzinena kucititsa manyazi.

13. Koma zinthu zonse potsutsika ndi kuunika, zionekera; pakuti conse cakuonetsa ciri kuunika.

14. Mwa ici anena, Khala maso wogona iwe, nuuke kwa akufa, ndi, po Kristu adzawala pa iwe.

15. Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;

16. akucita macawi, popeza masiku ali oipa,

17. Cifukwa cace musakhale opusa, koma dziwitsani cifuniro ca Ambuye nciani.

18. Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli citayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

19. ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira ndi kuyimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu;

20. ndi kuyamika Mulungu Atate masiku onse, cifukwa ca zonse, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu;

21. ndi kumverana wina ndi mnzace m'kuopa Kristu.

22. Akazi Inu, mverani amuna anu ainu eni, monga kumvera Ambuye.

Werengani mutu wathunthu Aefeso 5