2. ndi kuonetsera kudzicepetsa konse, ndi cifatso, ndi kuonetsera cipiriro, ndi kulolerana wina ndi mnzace, mwa cikondi;
3. ndi kusamalitsa kusunga umodzi wa Mzimu mwa cimangiriro ca mtendere.
4. Thupi limodzi ndi Mzimu mmodzi, monganso anakuitanani m'ciyembekezo cimodzi ca maitanidwe anu;
5. Ambuye mmodzi, cikhulupiriro cimodzi, ubatizo umodzi,
6. Mulungu mmodzi ndi Atate wa onse amene ali pamwamba pa onse, ndi mwa onse, ndi m'kati mwa zonse.