Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 3:6-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. kuti amitundu ali olowanyumbapamodzi ndi ife, ndi ziwalo zinzathu za thupilo, ndi oland ira nafe pamodzi palonjezano mwa Kristu Yesu, mwa Uthenga Wabino,

7. umene anandikhalitsa mtumiki wace monga mwa mphatso ya cisomo ca Mulungu, cimene anandipatsa ine, monga mwa, macitidwe a mphamvu yace.

8. Kwa ine wocepa ndi wocepetsa wa onse, oyera mtima anandipatsa cisomo ici, ndilalikire kwa amitundu cuma cosalondoleka ca Kristu;

9. ndi kuwalitsira onse adziwe makonzedwe a cinsinsico, cimene cinabisika ku yambira kale kale mwa Mulungu wolenga zonse;

10. kuti mu Eklesia azindikiritse tsopano kwa akulu ndi maulamuliro m'zakumwamba nzeru ya mitundu mitundu ya Mulungu,

11. monga mwa citsimikizo mtima ca nthawi za nthawi, cimene anacita mwa Kristu Yesu Ambuye wathu:

12. amene tiri naye cokhazikika mtima ndi ciyandiko eolimbika, mwa cikhulupiriro ca pa iye.

13. Mwa ici ndipempha kuti musade mtima, m'zisautso zanga cifukwa ca inu, ndiwo ulemerero wanu.

14. Cifukwa ca ici ndipinda maondo anga kwa Atate,

15. amene kucokera kwa iye pfuko lonse la m'mwamba ndi la padziko alicha dzina,

16. kuti monga mwa cuma ca ulemerero wace akulimbikitseni inu ndi mphamvu mwa Mzimu wace, m'kati mwanu,

Werengani mutu wathunthu Aefeso 3