Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 2:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. kuti akaonetsere m'nyengo zirinkudza cuma coposa ca cisomo cace, m'kukoma mtima kwa pa ife mwa Kristu Yesu.

8. Pakuti muli opulumutsidwa ndi cisomo cakucita mwa cikhulupiriro, ndipo ici cosacokera kwa inu: ciri mphatso ya Mulungu;

9. cosacokera kunchito, kuti asadzitamandire munthu ali yense.

10. Pakuti ife ndife cipango cace, olengedwa mwa Kristu Yesu, kucita nchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo.

Werengani mutu wathunthu Aefeso 2