Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 1:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Anatikonzeratu tilandiridwe ngati ana, a iye yekha mwa Yesu Kristu, monga umo kunakomera cifuniro cace,

6. kuti uyamikidwe ulemerero wa cisomo cace, cimene anaticitira ife kwaufulu mwa Wokondedwayo.

7. Tiri ndi maomboledwe mwa mwazi wace, cikhululukiro ca zocimwa, monga mwa kulemera kwa cisomo cace,

8. cimene anaticurukitsira ife m'nzeru zonse, ndi cisamaliro.

Werengani mutu wathunthu Aefeso 1