Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Timoteo 4:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti idzafika nthawi imene sadzalola ciphunzitso colamitsa; komatu poyabwa m'khutu adzadziuniikitsa aphunzitsi monga mwa zilakolako za iwo okha:

4. ndipo adzalubza dala pacoonadi, nadzapatukira kutsata nthanu zacabe.

5. Koma iwe, khala maso m'zonse, imva zowawa, cita nchito ya mlaliki wa Uthenga Wabwino, kwaniritsa utumiki wako.

6. Pakuti ndirimkuthiridwa nsembe tsopano, ndipo nthawi ya kumasuka kwanga yafika.

Werengani mutu wathunthu 2 Timoteo 4