Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Timoteo 2:7-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Lingirira cimene ndinena; pakuti Ambuye adzakupatsa cidziwitso m'zonse.

8. Kumbukila Yesu Kristu, wouka kwa akufa, wocokera m'mbeu ya Davide, monga mwa Uthenga Wabwino wanga;

9. m'menemo ndimva zowawa kufikira zomangira, monga wocita zoipa; koma mau a Mulungu samangika.

10. Mwa ici ndipirira zonse, cifukwa ca osankhika, kuti iwonso akapeze cipulumutsoeo ca mwa Kristu Yesu, pamodzi ndi ulemerero wosatha.

11. Okhulupirika mauwa: Pakuti ngati tidamwalira ndi iye, tidzakhalanso moyo ndi iye:

12. ngati ttpirira, tidzacitanso ufumu ndi iye: ngati timkana Iye, Iyeyunso adzatikana ife:

13. ngati tikhala osakhulupirika, Iyeyu akhala wokhulupirika; pakuti sakhoza kudzikana yekha.

14. Uwakumbutse izi, ndi kuwacitira umboni pamaso pa Ambuye, kuti asacite makani ndi mau osapindulitsa kanthu, koma ogwetsa iwo akumva.

15. Ucite cangu kudzionetsera kwa Mulungu wobvomerezeka, wanchito wopanda cifukwa ca kucita manyazi, wolunjika nao bwino mau a coonadi.

16. Koma pewa nkhani zopanda pace; pakuti adzapitirira kutsata cisapembedzo,

17. ndipo mau ao adzanyeka cironda; a iwo ali Humenayo ndi Fileto;

Werengani mutu wathunthu 2 Timoteo 2