5. Koma ngatinso wina ayesana nao m'makani a masewero, sambveka korona ngati sanayesana monga adapangana.
6. Wam'munda wogwiritsitsa nchitoyo ayenera akhale woyamba kulandira zipatsozoo
7. Lingirira cimene ndinena; pakuti Ambuye adzakupatsa cidziwitso m'zonse.
8. Kumbukila Yesu Kristu, wouka kwa akufa, wocokera m'mbeu ya Davide, monga mwa Uthenga Wabwino wanga;
9. m'menemo ndimva zowawa kufikira zomangira, monga wocita zoipa; koma mau a Mulungu samangika.
10. Mwa ici ndipirira zonse, cifukwa ca osankhika, kuti iwonso akapeze cipulumutsoeo ca mwa Kristu Yesu, pamodzi ndi ulemerero wosatha.
11. Okhulupirika mauwa: Pakuti ngati tidamwalira ndi iye, tidzakhalanso moyo ndi iye:
12. ngati ttpirira, tidzacitanso ufumu ndi iye: ngati timkana Iye, Iyeyunso adzatikana ife: