Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Atesalonika 1:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. ndi kwa inu akumva cisautso mpumulo pamodzi ndi ire, pa bvumbulutso la Ambuye Yesu wocokera Kumwamba pamodzi ndi angelo a mphamvu yace,

8. m'lawi lamoto, ndi kubwezera cilango kwa iwo osamdziwa Mulungu, ndi iwo osamvera Uthenga Wabwino wa Ambuye wathu Yesu;

9. amene adzamva cilango, ndico cionongeko cosatha cowasiyanitsa ku nkhope ya Ambuye, ndi ku ulemerero wa mphamvu yace,

10. pamene adzadza kudzalemekezedwa mwa oyera mtima ace, ndi kukhala wodabwizitsa mwa onse akukhulupirira (popeza munakhulupirira umboni wathu wa kwa inu) m'tsiku lija.

11. Kukatero tikupemphereraninso nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akakuyeseni inu oyenera kuitanidwa kwanu, nakakwaniritse comkomera conse, ndi nchito ya cikhulupiriro mumphamvu;

12. kuti dzina la Ambuye wathu Yesu lilemekezedwe mwa inu, ndi inu mwa iye, monga mwa cisomo ca Mulungu wathu ndi Ambuye Yesu Kristu.

Werengani mutu wathunthu 2 Atesalonika 1