Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 7:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pokhala nao tsono malonjezano amenewa, okondedwa, tidzikonzere tokha kuleka codetsa conse ca thupi ndi ca mzimu, ndi kutsirfza ciyero m'kuopa Mulungu.

2. Tipatseni malo; sitinamcitira munthu cosalungama, sitinaipsa munthu, sitinacenjerera munthu.

3. Sindinena ici kuti ndikutsutseni: pakuti ndanena kale kuti muli mu mitima yathu, kuti tife limodzi ndi kukhala ndi moyo limodzi.

4. Ndilimbika mtima kwambiri pakunena nanu, kudzitamandira kwanga cifukwa ca inu nkwakukuru; ndidzazidwa naco citonthozo, ndisefukira naco cimwemwe m'cisautso cathu conse.

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 7