Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 6:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo a ocita naye pamodzi tidandauliranso kuti musalandire cisomo ca Mulungu kwacabe inu,

2. (pakuti anena,M'nyengo yolandiridwa ndinamva iwe,Ndipo m'tsiku la cipulumutso ndinakuthandiza;Taonani, tsopano ndiyo nyengo yabwino yolandiridwa, taonani, tsopano ndilo tsiku la cipulumutso);

3. osapatsa cokhumudwitsa konse m'cinthu ciri conse, kuti utumikiwo usanenezedwe;

4. koma m'zonse tidzitsimikfzira ife tokha monga atumiki a Mulungu, m'kupirira kwambiri, m'zisautso, m'zikakamizo, m'zopsinja,

5. m'mikwingwirima, m'ndende, m'mapokoso, m'mabvutitso, m'madikiro, m'masalo a cakudya;

6. m'mayeredwe, m'cidziwitso, m'cilekerero, m'kukoma mtima, mwa Mzimu Woyera, m'cikondi cosanyenga;

7. m'mau a coonadi, mu mphamvu ya Mulungu; mwa camuna ca cilungamo kulamanja ndi kulamanzere,

8. mwa ulemerero, mwa mnyozo, mwa mbiri yoipa ndi mbiri yabwino; mongaosoceretsa, angakhale ali oona;

9. monga osadziwika, angakhale adziwika bwino; monga alinkufa, ndipo taonani, tiri ndi moyo; monga olangika, ndipo osaphedwa;

10. monga akumva cisoni, koma akukondwera nthawi zonse; monga aumphawi, lroma akulemeretsa ambiri; mensa okhala opanda-kanthu, ndipo akhala nazo zinthu zonse.

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 6