Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 11:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. ndinalanda za Mipingo yina, ndi kulandira kwa iwo kulipira kuti ndikatumikire inu;

9. ndipo pakukhala nanu, ndi kusowa, sindinasaukitsa munthu ali yense; pakuti abale akucokera ku Makedoniya, anakwaniritsa kusowa kwanga; ndipo m'zonse ndinacenjera ndekha, ndisalemetse inu, ndipo ndidzacenjerapo.

10. Coonadi ca Kristu ciri mwa ine, kuti kudzitamandira kumene sikudzaletsedwa kwa ine mu mbali za Akaya,

11. Cifukwa ninji? Cifukwa sindikonda inu kodi? Adziwa Mulungu.

12. Koma cimene ndicita, ndidzacitanso, kuti ndikawadulire cifukwa iwo akufuna cifukwa; kuti m'mene adzitamandiramo, apezedwe monganso ife.

13. Pakuti otere ali atumwi onyenga, ocita ocenjerera, odzionetsa ngati atumwi a Kristu,

14. Ndipo kulibe kudabwa; pakuti Satana yemwe adzionetsa ngati mngelo wa kuunika.

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 11