Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Yohane 2:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. koma iye amene akasunga mau ace, mwa iyeyu zedi cikondi ca Mulungu cathedwa. M'menemo tizindikira kuti tiri mwa iye;

6. iye wakunena kuti akhala mwa Iye, ayeneranso mwini wace kuyenda monga anayenda Iyeyo.

7. Okondedwa, sindikulemberani lamulo latsopano, komatu lamulo lakale limene munali nalo kuyambira pa ciyambi; Lamulo Iakaielo ndilo mau amene mudawamva.

8. Ndikulemberaninso lamulo latsopano, ndico cimene ciri coona mwa iye ndi mwa inu; kuti mdima ulinkupita, ndi kuunika koona kwayamba kuwala,

9. iye amene anena kuti ali m'kuunika, namuda mbale wace, ali mumdima kufikira tsopane lino.

Werengani mutu wathunthu 1 Yohane 2