17. Ndipo dziko lapansi lipita, ndi cilakolako cace; koma iye amene acita cifuniro ca Mulungu akhala ku nthawi yonse.
18. Ana inu, ndi nthawi yorsirtza iyi; ndipo monga mudamva kuti wokana. Krisru akudza, ngakhale tsopano alipo okana Kristu ambiri; mwa ici tizindikira kuti ndi nthawi yotsirizira iyi.
19. Anaturuka mwa ife, komatu sanali a ife; pakuti akadakhala a ife akadakhalabe ndi ife, koma kudatero 1 kuti aonekere kutr sali onse a ife.
20. Ndipo 2 inu muti nako kudzoza kocokera kwa Woyerayo, ndipo 3 mudziwa zonse.
21. Sindinakulemberam cifukwa simudziwa coonadi, koma cifukwa muddziwa, ndi cifukwa kulibe bodza locokera kwa coonadi.
22. 4 Wabodza ndani, koma iye wokanayo kuti Yesu siali Kristu? iye ndiye wokana Kristu, amene akana Atate ndi Mwana.
23. 5 Yense wakukana Mwana, alibe Atate; wobvomereza Mwana ali ndi Atatenso.
24. Koma inu, cimene munacimva kuyambira paciyambi cikhale mwa Inu, 6 Ngari cikhala mwa inu cimene mudacimva kuyambira paciyambi, inunso mudzakhalabe mwa Mwana, ndi mwa Atate.
25. Ndipo 7 ili ndi lonjezano iye anatiloniezera ife, ndiwo moyo wosatha.