Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Timoteo 5:1-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mkulu usamdzudzule, komatu umdandaulire ngati atate; anyamata ngati abale;

2. akazi akulu ngati amai; akazi ang'ono ngati alongo, m'kuyera mtima konse.

3. Citira ulemu amasiye amene ali amasiye ndithu.

4. Koma ngati wamasiye wina ali nao ana kapena adzukulu, ayambe aphunzire iwo kucitira ulemu a m'banja lao, ndi kubwezera akuwabala; pakuti ici ncolandirika pamaso pa Mulungu.

5. Koma iye amene ali wamasiye ndithu, nasiyidwa yekha, ayembekezera Mulungu, nakhalabe m'mapembedzo ndi mapemphero usiku ndi usana.

6. Koma iye wakutsata zomkondweretsa, adafa pokhala ali ndi moyo,

7. Ndipo izi ulamulire, kuti akhale opanda ciremao

8. Koma ngati wina sadzisungiratu mbumba yace ya iye yekha, makamaka iwo a m'banja lace, wakana cikhulupiriro iye, ndipo aipa koposa wosakhulupira.

9. Asawerengedwe wamasiye ngati sanafikire zaka makumi asanu ndi limodzi, atakhala mkazi wa mwamuna mmodzi,

10. wa mbiri ya nchito zabwino; ngati walera ana, ngati wacereza alendo, ngati adasambitsa mapazi a nzera mtima, ngati wathapdiza osautsidwa, ngati anatsatadi nchito zonse zabwino.

11. Koma amasiyeang'ono uwakane; pakuti pamene ayambakumcitira Kristu cipongwe afuna kukwatiwa;

12. pokhala naco citsutso, popeza adataya cikhulupiriro cao coyamba.

13. Ndipo aphunziraponso kucita ulesi, aderuderu; koma osati ulesi wokha, komatunso alankhula zopanda pace, nacita mwina ndi mwina, olankhula zosayenera.

14. Cifukwa cace nditi akwatiwe amasiye ang'ono, nabale ana, naweruzire nyumba, osapatsa cifukwa kwa mdaniyo cakulalatira;

15. pakuti adayamba enakupatuka ndi kutsata Satana.

16. Ngati mkazi wina wokhulupira ali nao amasiye, iye awathandize, ndipo Mpingowo usalemedwe; kuti uthandize iwo amene ali amasiye ndithu.

17. Akuru akuweruza bwino ayesedwe oyenera ulemu wowirikiza, makamaka iwo akucititsa m'mau ndi m'ciphunzitso.

18. Pakuti malembo ati, Usapunamiza ng'ombe yopuntha tirigu. Ndipo, Wogwira nchito ayenera kulipira kwace.

19. Pa mkulu usalandire comnenera, koma pakhale mboni ziwiri kapena zitatu.

Werengani mutu wathunthu 1 Timoteo 5