Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Petro 1:16-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. popeza kwalembedwa, Muzikhala oyera mtima, pakuti Ine ndine woyera mtima.

17. Ndipo mukamuitana ngati Alate, iye amene aweruza monga mwa nchito ya yense, wopanda tsankhu, khalani ndi mantha nthawi ya cilendo canu;

18. podziwa kuti simunaomboledwa ndi zobvunda, golidi ndi siliva, kusiyana nao makhalidwe anu acabe ocokera kwa makolo anu:

19. koma 1 ndi mwazi wa mtengo wace wapatali 2 monga wa mwana wa nkhosa wopanda cirema, ndi wopanda banga, ndiwo mwazi wa Kristu:

20. 3 amene anazindikirikatu lisanakhazikike dziko lapansi, koma anaonetsedwa pa citsiriziro ca nthawi,

21. cifukwa ca inu amene mwa rye mukhulupirira Mulungu 4 wakwnuukitsa iye kwa akufa, ndi kumpatsa iye ulemerero; kotero kuti cikhulupiriro canu ndi ciyembekezo canu cikhale pa Mulungu.

22. Popeza 5 mwayeretsa moyo wanu pakumvera coonadi kuti 6 mukakonde abale ndi cikondi cosanyenga, mukondane kweni kweni kucokera kumtima;

23. 7 inu amene mudabadwanso, osati ndi mbeu yofeka, komatu yosaola, mwa mau a Mulungu amoyo ndi okhalitsa.

24. Popeza,8 Anthu onse akunga udzu,Ndi ulemerero waowonse ngad duwa la udzu.Udzuwo ungotota, ndi duwa lace lingogwa;

25. 9 Koma Mau a Mulungu akhala cikhalire.Ndipo 10 mau olalikidwa kwa Inu ndi jawo.

Werengani mutu wathunthu 1 Petro 1