Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Atesalonika 5:14-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma tidandaulira inu abale, yambirirani ampwayi, limbikitsani amantha mtima? cirikizani ofok a, mukhale oleza mtima pa onse.

15. Penyani kuti wina asabwezere coipa womcitira coipa; komatu nthawi zonse mutsatire cokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.

16. Kondwerani nthawi zonse;

17. Pempherani kosaleka;

18. M'zonse yamikani; pakuti ici ndi cifuniro ca Mulungu ca kwa inu, mwa Kristu Yesu.

19. Musazime Mzimuyo;

20. Musanyoze maaenero;

21. Yesani zonse; sungani cokomaco,

22. Mupewe maonekedwe onse a coipa.

23. Ndipo Mulungu wa mtendere yekha ayeretse inu konsekonse; ndipo mzimu wanu ndi moyo wanu ndi thupi lanu zisungidwe zamphumphu, zopanda cirema pa kudza kwace kwa: Ambuye wathu Yesu Kristu.

24. Wakuitana inu ali wokhulupirika, amenensoadzacicita.

Werengani mutu wathunthu 1 Atesalonika 5