Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Atesalonika 5:11-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mwa ici cenjezanani, ndipo mangiriranani wina ndi mnzace, monganso mumacita,

12. Koma, abale, tikupemphani, dziwani iwo akugwiritsa nchito mwa inu, nakhala akulu anu mwa Ambuye, nakuyatnbirirani inu;

13. ndipo muwacitire ulemu woposatu mwa cikondi, cifukwa ca nchito yao. Khalani mumtendere mwa inu nokha.

14. Koma tidandaulira inu abale, yambirirani ampwayi, limbikitsani amantha mtima? cirikizani ofok a, mukhale oleza mtima pa onse.

15. Penyani kuti wina asabwezere coipa womcitira coipa; komatu nthawi zonse mutsatire cokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.

16. Kondwerani nthawi zonse;

17. Pempherani kosaleka;

18. M'zonse yamikani; pakuti ici ndi cifuniro ca Mulungu ca kwa inu, mwa Kristu Yesu.

19. Musazime Mzimuyo;

20. Musanyoze maaenero;

21. Yesani zonse; sungani cokomaco,

22. Mupewe maonekedwe onse a coipa.

23. Ndipo Mulungu wa mtendere yekha ayeretse inu konsekonse; ndipo mzimu wanu ndi moyo wanu ndi thupi lanu zisungidwe zamphumphu, zopanda cirema pa kudza kwace kwa: Ambuye wathu Yesu Kristu.

24. Wakuitana inu ali wokhulupirika, amenensoadzacicita.

25. Abale, z tipempherereni ife.

26. 1 Lankhulani abale onse ndi cipsompsono copatulika.

27. Ndikulumbirirani pa Ambuye kuti 2 kalatayu awerengedwe kwa abale onse.

Werengani mutu wathunthu 1 Atesalonika 5