Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Atesalonika 4:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pakuti Mulungu sanaitana ife titsate cidetso, koma ciyeretso.

8. Cifukwa cace iye wotaya ici, sataya munthu, komatu Mulungu, wakupatsa Mzimu wace Woyera kwa inu.

9. Koma kunena za cikondano ca pa abale sikufunika kuti akulembereni; pakuti wakukuphunzitsani ndi Mulungu, kuti mukondane wina ndi mnzace;

10. pakutinso munawacitira ici abale onse a m'Makedoniya lonse. Koma tikudandaulirani, abale, mueurukireko koposa,

11. ndi kuti muyesetse kukhala cete ndi kucita za inu eni ndi kugwira nchito ndi manja anu, monga tinakuuzani;

12. kuti mukayende oona mtima pa iwo a kunja, ndi kukhala osasowa kanthu.

13. Koma sitifuna, abale, kuti mukhale osadziwa za iwo akugona; kuti mungalire monganso otsalawo, amene alibe ciyembekezo.

14. Pakuti ngati tikhulupirira kuti Yesu adamwalira, nauka, koteronso Mulungu adzatenga pamodzi ndi iye iwo akugona mwa Yesu.

15. Pakuti ici tinena kwa inu m'mau a Ambuye, kuti ife okhala ndi moyo, otsalira kufikira kufikanso kwa Ambuye, sitidzatsogolera ogonawo.

16. Pakuti Ambuye adzatsika Kumwamba mwini yekha ndi mpfuu, ndi mau a mngelo wamkuru, ndi lipenga la Mulungu; ndipo akufa mwa Ambuye adzayamba kuuka;

Werengani mutu wathunthu 1 Atesalonika 4