Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Atesalonika 3:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. cifukwa ca ici tasangalala pa inu, abale, m'kupsinjika kwathu konse ndi cisautso cathu conse, mwa cikhulupiriro canu;

8. pakuti tsopano tiri ndi moyo, ngati inu mucirimika mwa Ambuye.

9. Pakuti tikhoza kubwezera kwa Mulungu ciyamiko canji cifukwa ca inu, pa cimwemwe conse tikondwera naco mwa inu pamaso pa Mulungu wathu;

10. ndi kucurukitsa mapemphero athu usiku ndi usana kuti tikaone nkhope yanu, ndi kukwaniritsa zoperewera pa cikhulupiriro canu?

11. Koma Mulungu Atate wathu mwini yekha, ndi Ambuye wathu Yesu atitsogolere m'njira yakufika kwa inu;

12. koma Ambuye akukulitseni inu, nakueurukitseni m'cikondano wina kwa mnzace ndi kwa anthu onse, monganso ife titero kwa inu;

13. kuti akakhazikitse mitima yanu yopanda cifukwa m'ciyero pamaso pa Mulungu Atate wathu, pakufika Ambuye wathu Yesu pamodzi ndi oyera mtima ace onse.

Werengani mutu wathunthu 1 Atesalonika 3