Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 9:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Kapena cilamulo sieinenanso zomwezo?

9. Pakuti m'cilamulo ca Mose mwalembedwa, Usapunamitsa ng'ombe pakupuntha iyo dzinthu. Kodi Mulungu asamalira ng'ombe?

10. Kapena acinena ici konse konse cifukwa ca ife? Pakuti, cifukwa ca ife kwalembedwa: popeza wolima ayenera kulima mwa ciyembekezo, ndi wopunthayo acita mwa ciyembekezo ca kugawana nao.

11. Ngati takufeserani inu zauzimu, kodi ncacikuru ngati ife tituta za thupi lanu?

12. Ngati ena ali nao ulamuliro umene pa inu, si ife nanga koposa? Koma sitinacita nao ulamuliro umene; koma timalola zonse, kuti tingacite cocedwetsa kwa Uthenga Wabwino wa Kristu,

13. Kodi simudziwa kuti iwo akutumikira za kacisi amadya za m'Kacisi, ndi iwo akuimirira guwa la nsembe, agawana nalo guwa la nsembe?

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 9