Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 9:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Kodi tiribe ulamuliro wa kudya ndi kumwa?

5. Kodi tiribe ulamuliro wakuyendayenda naye mkazi, ndiye mbale, monganso atumwi ena, ndi abale a Ambuye, ndi Kefa?

6. Kapena kodi ife tokha, Bamaba ndi ine, tiribe ulamuliro wakusagwira nchito?

7. Msilikari ndani acita nkhondo, nthawi iriyonse, nadzifunira zace yekha? Aoka mipesa ndani, osadya cipatso cace? Kapena aweta gulu ndani, osadyamkaka wace wa gululo? Kodi ndilankhula izi monga mwa anthu?

8. Kapena cilamulo sieinenanso zomwezo?

9. Pakuti m'cilamulo ca Mose mwalembedwa, Usapunamitsa ng'ombe pakupuntha iyo dzinthu. Kodi Mulungu asamalira ng'ombe?

10. Kapena acinena ici konse konse cifukwa ca ife? Pakuti, cifukwa ca ife kwalembedwa: popeza wolima ayenera kulima mwa ciyembekezo, ndi wopunthayo acita mwa ciyembekezo ca kugawana nao.

11. Ngati takufeserani inu zauzimu, kodi ncacikuru ngati ife tituta za thupi lanu?

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 9