Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 9:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kodi sindine mfulu? Kodi slndine mtumwi? Kodi sindinaona Yesu Ambuye wathu? Kodi simuli inu nchito yanga mwa Ambuye?

2. Ngati sindiri mtumwi kwa ena, komatu ndiri kwa inu; pakuti cizindikilo ca utumwi wanga ndi inu mwa Ambuye.

3. Codzikanira canga kwa iwoamene andifunsa ine ndi ici:

4. Kodi tiribe ulamuliro wa kudya ndi kumwa?

5. Kodi tiribe ulamuliro wakuyendayenda naye mkazi, ndiye mbale, monganso atumwi ena, ndi abale a Ambuye, ndi Kefa?

6. Kapena kodi ife tokha, Bamaba ndi ine, tiribe ulamuliro wakusagwira nchito?

7. Msilikari ndani acita nkhondo, nthawi iriyonse, nadzifunira zace yekha? Aoka mipesa ndani, osadya cipatso cace? Kapena aweta gulu ndani, osadyamkaka wace wa gululo? Kodi ndilankhula izi monga mwa anthu?

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 9