1. Kodi sindine mfulu? Kodi slndine mtumwi? Kodi sindinaona Yesu Ambuye wathu? Kodi simuli inu nchito yanga mwa Ambuye?
2. Ngati sindiri mtumwi kwa ena, komatu ndiri kwa inu; pakuti cizindikilo ca utumwi wanga ndi inu mwa Ambuye.
3. Codzikanira canga kwa iwoamene andifunsa ine ndi ici:
4. Kodi tiribe ulamuliro wa kudya ndi kumwa?
5. Kodi tiribe ulamuliro wakuyendayenda naye mkazi, ndiye mbale, monganso atumwi ena, ndi abale a Ambuye, ndi Kefa?