Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 6:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Kodi simudziwa kuti tidzaweruza angelo? koposa kotani nanga zinthu za moyo uno?

4. Cifukwa cace, ngati muli nayo mirandu ya zinthu za moyo uno, kodi muweruzitsa iwo amene ayesedwa acabe mu Mpingo?

5. Ndinena ici kukucititsani inu manyazi. Kodi nkutero kuti mwa inu palibe mmodzi wanzeru, amene adzakhoza kuweruza pa abale,

6. koma mbale anena mlandu ndi mbale, ndikotu kwa osakhulupira?

7. Koma pamenepo pali cosowa konse konse mwa inu, kuti muli nayo mirandu wina ndi mnzace. Cifukwa ninji simusankhula kulola kuipsidwa? simusankhula cifukwa ninji kulolakunyengedwa?

8. Koma muipsa, nimunyenga, ndipo mutero nao abale anu.

9. Kapenasimudziwa kuti osalungama sadzalandira ufumu wa Mulungu? Musasoceretsedwe; adama, kapena opembedza mafano, kapena acigololo, kapena olobodoka ndi zoipa, kapena akudziipsa ndi amuna,

10. kapena ambala, kapena osirira, kapena oledzera, kapena olalatira, kapena olanda, sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

11. Ndipo ena ainu munali otere; koma munasambitsidwa, koma munayeretsedwa, koma munayesedwa olungama, m'dzina la Ambuye Yesu Kristu, ndi mwa Mzimu wa Mulungu wathu.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 6