Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 6:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. koma Mulungu anaukitsa Ambuye, ndiponso adzaukitsa ife mwa mphamvu yace.

15. Kodi simudziwa kuti matupi anu ali ziwalo za Kristu? cifukwa cace ndidzatenga ziwalo za Kristu kodi, ndi kuziyesa ziwalo za mkazi waciwerewere? Msatero iai.

16. Kapena simudziwa kuti iye wophatikidwa ndi mkazi waciwerewere ali thupi limodzi? Pakuti, awiriwo, ati, adzakhala thupi limodzi.

17. Koma iye wophatikidwa ndi Ambuye ali mzimu umodzi.

18. Thawani dama. Cimo liri lonse munthu akalicita liri kunja kwa thupi; koma waciwerewere acimwira thupi lace la iye yekha.

19. Kapena simudziwa kuti thupi lanu liri kacisi wa Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene muli naye kwa Mulungu? Ndipo simukhala a inu nokha.

20. Pakuti munagulidwa ndi mtengo wace wapatali; cifukwa cace lemekezani Mulungu m'thupi lanu.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 6