Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 6:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Zinthu zonse ziloledwa kwa ine; koma si zonse zipindula, Zinthu zonse ziloledwa kwa ine, koma sindidzalamulidwa naco cimodzi.

13. Zakudya ndizo za mimba, ndi mimba ndiyo ya zakudya; koma Mulungu adzathera iyi ndi izi. Koma thupi siliri la cigololo, koma la Ambuye, ndi Ambuye wa thupi;

14. koma Mulungu anaukitsa Ambuye, ndiponso adzaukitsa ife mwa mphamvu yace.

15. Kodi simudziwa kuti matupi anu ali ziwalo za Kristu? cifukwa cace ndidzatenga ziwalo za Kristu kodi, ndi kuziyesa ziwalo za mkazi waciwerewere? Msatero iai.

16. Kapena simudziwa kuti iye wophatikidwa ndi mkazi waciwerewere ali thupi limodzi? Pakuti, awiriwo, ati, adzakhala thupi limodzi.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 6