Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 15:37-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. ndipo cimene ufesa, sufesa thupi limene lidzakhala, koma mbeu yokhakapenaya tirigu kapena ya, mtundu wina;

38. koma Mulungu iaipatsa thupi mongaafuna; ndi, kwa mbeu yonse thupi lace lace.

39. Nyama yonse siiri imodzimodzi; koma yinandi Ya anthu, ndi yina ndiyo nyama ya zoweta, ndi yina ndiyo nyama ya mbalame, ndi yina ya nsomba.

40. Palinso matupi am'mwamba, ndi matupi apadziko: koma ulemerero wa lam'mwamba ndi wina, ndi ulemerero wa lapadziko ndi winanso.

41. Kuli ulemerero wa dzuwa, ndi ulemerero wina wa mwezi, ndi ulemerero wina wa nyenyezi; pakuti nyenyezi isiyana ndi nyenyezi m'ulemerero.

42. 9 Comweconso kudzakhala kuuka kwa akufa. Lifesedwa m'cibvundi, liukitsidwa m'cisabvundi;

43. 10 lifesedwa m'mnyozo, liukitsidwa m'ulemerero; lifesedwa m'cifoko, liukitsidwa mumphamvu;

44. lifesedwa thupi Iacibadwidwe, liukitsidwa thupi lauzimu. Ngati pali thupi Iacibadwidwe, palinso lauzimu.

45. Koteronso kwalembedwa, 11 Munthu woyamba, Adamu, anakhala mzimu wamoyo. 12 Adamu wotsirizayo anakhala mzimu wakulenga moyo.

46. Koma cauzimu siciri coyamba, koma cacibadwidwe; pamenepo cauzimu.

47. 13 Munthu woyambayo ali wapansi, wanthaka. Munthu waciwiri ali wakumwamba.

48. 14 Monga wanthakayo, ateronso anthaka; ndi monga wakumwamba, ateronso akumwamba.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 15