Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 15:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Koma yense m'dongosolo lace la iye yekha, cipatso coundukula Kristu, pomwepo iwo a Kristu, pa kubwera kwace.

24. Pomwepo pali cimariziro, pamene adzapereka ufumu kwa Mulungu, ndiye Atate, atatha kuthera ciweruzo conse, ndi ulamuliro wonse, ndi mphamvu yomwe.

25. Pakuti ayenera kucita ufumu kufikira ataika adani onse pansi pa mapazi ace.

26. Mdani wotsiriza amene adzathedwa ndiye imfa.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 15