Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 15:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pakuti monga imfa inadza mwa munthu, kuuka kwa akufa kunadzanso mwa munthu.

22. Pakuti mongamwa Adamu onse amwalira, coteronso mwa Kristu onse akhalitsidwa ndi moyo.

23. Koma yense m'dongosolo lace la iye yekha, cipatso coundukula Kristu, pomwepo iwo a Kristu, pa kubwera kwace.

24. Pomwepo pali cimariziro, pamene adzapereka ufumu kwa Mulungu, ndiye Atate, atatha kuthera ciweruzo conse, ndi ulamuliro wonse, ndi mphamvu yomwe.

25. Pakuti ayenera kucita ufumu kufikira ataika adani onse pansi pa mapazi ace.

26. Mdani wotsiriza amene adzathedwa ndiye imfa.

27. Pakuti Iye anagonjetsa zonse pansi pa mapazi ace. Koma pamene anena kutizonse zagonjetsedwa, kuzindikirika kuti sawerengapo Iye amene anagonjetsa zonsezo kwa Iye.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 15